Add parallel Print Page Options

Kumbukirani masiku amakedzana;
    ganizirani za mibado yakalekale.
Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza,
    akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.
Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo,
    pamene analekanitsa anthu onse,
anayikira malire anthu onse
    molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.
Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake,
    Yakobo ndiye cholowa chake.

10 Anamupeza mʼchipululu,
    ku malo owuma ndi kopanda kanthu.
Anamuteteza ndi kumusamalira;
    anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,
11 ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake
    nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake,
chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo
    ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.
12 Yehova yekha ndiye anamutsogolera;
    popanda thandizo la mulungu wachilendo.

13 Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko
    ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda.
Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe,
    ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,
14 pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa,
    ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi,
pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani
    ndiponso tirigu wabwino kwambiri.
Munamwa vinyo wa thovu lofiira.

15 Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira;
    atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi.
Anasiya Mulungu amene anamulenga
    ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.
16 Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo
    ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.
17 Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu,
    milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe,
    milungu yongobwera kumene,
    milungu imene makolo anu sankayiopa.
18 Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani;
    munayiwala Mulungu amene anakubalani.

Read full chapter