Deuteronomo 32:7-18
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
7 Kumbukirani masiku amakedzana;
ganizirani za mibado yakalekale.
Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza,
akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.
8 Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo,
pamene analekanitsa anthu onse,
anayikira malire anthu onse
molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.
9 Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake,
Yakobo ndiye cholowa chake.
10 Anamupeza mʼchipululu,
ku malo owuma ndi kopanda kanthu.
Anamuteteza ndi kumusamalira;
anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,
11 ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake
nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake,
chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo
ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.
12 Yehova yekha ndiye anamutsogolera;
popanda thandizo la mulungu wachilendo.
13 Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko
ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda.
Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe,
ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,
14 pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa,
ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi,
pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani
ndiponso tirigu wabwino kwambiri.
Munamwa vinyo wa thovu lofiira.
15 Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira;
atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi.
Anasiya Mulungu amene anamulenga
ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.
16 Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo
ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.
17 Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu,
milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe,
milungu yongobwera kumene,
milungu imene makolo anu sankayiopa.
18 Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani;
munayiwala Mulungu amene anakubalani.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.