Genesis 11:24-32
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
24 Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera. 25 Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
26 Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
Mibado Yochokera mwa Tera
27 Nayi mibado yochokera mwa Tera.
Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti. 28 Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira. 29 Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani. 30 Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
31 Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
32 Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.
Read full chapter
Yoswa 24:2
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
2 Yoswa anati kwa anthu onse, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Kalekale makolo anu, kuphatikiza Tera, abambo a Abrahamu ndi Nahori ankakhala kutsidya kwa Mtsinje ndipo ankapembedza milungu ina.
Read full chapter
1 Mbiri 1:26
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
26 Serugi, Nahori, Tera
Luka 3:34
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
34 mwana wa Yakobo,
mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu,
mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.