Amosi 8:1-3
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Dengu la Zipatso Zakupsa
8 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: dengu la zipatso zakupsa. 2 Iye anandifunsa kuti, “Amosi nʼchiyani ukuona?”
Ine ndinayankha kuti, “Dengu la zipatso zakupsa.”
Ndipo Yehova anati kwa ine, “Nthawi yachimaliziro yawakwanira anthu anga Aisraeli; sindidzawakhululukiranso.
3 “Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akulengeza kuti, “Nyimbo za mʼNyumba ya Mulungu zidzasanduka kulira kofuwula. Mitembo ya anthu idzachuluka, ndipo adzayiponya ponseponse! Kudzangoti zii!”
Read full chapterThe Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.