Add parallel Print Page Options

Mawu a Elihu

32 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama. Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga. Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa. Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo. Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.

Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati:

“Ine ndine wamngʼono,
    inuyo ndinu akuluakulu,
nʼchifukwa chake ndimaopa,
    ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula;
    anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu,
    mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
Si okalamba amene ali ndi nzeru,
    si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.

10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni;
    inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
11 Ndadikira nthawi yonseyi,
    ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula,
pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
12     ineyo ndinakumvetseranidi.
Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu;
    palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru;
    Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine,
    ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.

15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso;
    mawu awathera.
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano,
    pakuti angoyima phee wopanda yankho?
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano;
    nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri,
    ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo,
    ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike;
    ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense,
    kapena kuyankhula zoshashalika,
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika,
    Mlengi wanga akanandilanga msanga.”

33 “Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga;
    mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
Tsopano ndiyamba kuyankhula;
    mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama;
    pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba,
    mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
Mundiyankhe ngati mungathe;
    konzekani tsopano kuti munditsutse.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu;
    nanenso ndinachokera ku dothi.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi,
    Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.

“Koma inu mwayankhula ine ndikumva,
    ndamva mawu anuwo onena kuti,
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo;
    ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo;
    Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo,
    akulonda mayendedwe anga onse.’

12 “Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi,
    pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye
    kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana,
    ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku,
    pamene anthu ali mʼtulo tofa nato
    pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 amawanongʼoneza mʼmakutu
    ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 kumuchotsa munthu ku zoyipa,
    ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 kumulanditsa munthu ku manda,
    kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.

19 “Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake,
    nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya,
    ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 Thupi lake limawonda
    ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 Munthuyo amayandikira ku manda,
    moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.

23 “Koma patakhala mngelo ngati mthandizi,
    mmodzi mwa ambirimbiri oterewa,
    adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 kudzamukomera mtima ndi kunena kuti,
    ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda;
    ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana;
    ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa.
    Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe
    ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti,
    ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama,
    koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda,
    ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’

29 “Mulungu amachita zonsezi kwa munthu
    kawirikawiri,
30 kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda,
    kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.

31 “Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere;
    khalani chete kuti ndiyankhule.
32 Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni;
    yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 Koma ngati sichoncho, mundimvere;
    khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

34 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,

“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru;
    tcherani khutu inu anthu ophunzira.
Pakuti khutu limayesa mawu
    monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera;
    tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.

“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa,
    koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
Ngakhale ndine wolungama mtima,
    akundiyesa wabodza;
ngakhale ndine wosachimwa,
    mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani,
    amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa;
    amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu
    poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’

10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu.
    Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe,
    Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake;
    Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa,
    kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani?
    Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo
    oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu
    ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.

16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi;
    mvetserani zimene ndikunena.
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira?
    Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’
    ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
19 Iye sakondera akalonga
    ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka,
    pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku;
    anthu amachita mantha ndipo amamwalira;
    munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.

21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu;
    amaona mayendedwe ake onse.
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani
    kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu,
    kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu
    ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo
    amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo,
    pamalo pamene aliyense akuwaona;
27 Chifukwa anasiya kumutsata
    ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake,
    kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa?
    Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe?
Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
30     kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza,
    kuti asatchere anthu misampha.

31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti,
    ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona
    ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira,
    pamene inu mukukana kulapa?
Chisankho nʼchanu, osati changa;
    tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.

34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana,
    anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru;
    mawu ake ndi opanda fundo.’
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto
    chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira;
    amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu,
    ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”

35 Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,

“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza?
    Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani,
    ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’

“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu
    pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
Yangʼanani kumwamba ndipo muone
    mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani?
    Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani?
    Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo,
    ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.

“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa;
    akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
10 Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga,
    amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
11 amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi
    ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
12 Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye
    chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
13 Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake;
    Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
14 Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti
    Iye saona zimene zikuchitika.
Iye adzaweruza molungama ngati
    inu mutamudikira
15 ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango,
    zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
16 abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake,
    mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”

36 Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:

“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani
    kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali;
    ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
Ndithudi mawu anga si abodza;
    wanzeru zangwiro ali ndi inu.

“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu;
    Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo
    koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama;
    amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu
    ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo,
    ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
Iye amawafotokozera zomwe anachita,
    kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake
    ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira,
    adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere,
    adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 Koma ngati samvera,
    adzaphedwa ndi lupanga
    ndipo adzafa osadziwa kanthu.

13 “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo;
    akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Amafa akanali achinyamata,
    pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo;
    Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.

16 “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso,
    kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani,
    kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu;
    chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma;
    musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Kodi chuma chanu
    kapena mphamvu zanu zonse
    zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Musalakalake kuti usiku ubwere,
    pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo,
    chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.

22 “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu.
    Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite,
    kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Kumbukirani kutamanda ntchito zake
    zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 Anthu onse amaziona ntchitozo;
    anthuwo amaziona ali kutali.
26 Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe!
    Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.

27 “Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo,
    timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 mitambo imagwetsa mvulayo
    ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera,
    momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse,
    zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu
    ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani,
    ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho;
    ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.

37 “Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso
    ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake,
    kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse
    ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka.
    Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero.
Pamene wabangula,
    palibe chimene amalephera kuchita.
Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa
    Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’
    ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake.
    Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
Zirombo zimakabisala
    ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake,
    kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
10 Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi
    ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
11 Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula,
    amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
12 Mulungu amayendetsa mitamboyo
    mozungulirazungulira dziko lonse lapansi
    kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
13 Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu,
    kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.

14 “Abambo Yobu, tamvani izi;
    imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
15 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo
    ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
16 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo,
    ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
17 Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta
    pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
18 kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo
    limene ndi lolimba ngati chitsulo?

19 “Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye;
    sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
20 Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu?
    Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
21 Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa,
    ndi kunyezimira mlengalenga,
    kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
22 Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto;
    Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
23 Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa;
    pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
24 Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri,
    kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”