Add parallel Print Page Options

24 “Inu ana aakazi a Israeli,
    mulireni Sauli,
amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa,
    amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.

25 “Taonani amphamvu agwa ku nkhondo!
    Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
26 Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani,
    unali wokondedwa kwambiri kwa ine.
Chikondi chako pa ine chinali chopambana,
    chopambana kuposa chikondi cha akazi.

27 “Taonani amphamvu agwa!
    Zida zankhondo zawonongeka!”

Read full chapter