2 Samueli 1:24-27
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
24 “Inu ana aakazi a Israeli,
mulireni Sauli,
amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa,
amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
25 “Taonani amphamvu agwa ku nkhondo!
Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
26 Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani,
unali wokondedwa kwambiri kwa ine.
Chikondi chako pa ine chinali chopambana,
chopambana kuposa chikondi cha akazi.
27 “Taonani amphamvu agwa!
Zida zankhondo zawonongeka!”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.