Genesis 5:18-24
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
18 Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki. 19 Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 20 Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.
21 Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela. 22 Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 23 Zaka zonse za Enoki zinali 365. 24 Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.
Read full chapterThe Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.